Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 38:1-7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 38 Ndiyeno anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa a mthethe. Guwalo linali lofanana muyezo wake mbali zake zonse 4, mulitali linali mamita awiri* ndipo mulifupi linalinso mamita awiri. Kutalika kwake kuchokera pansi mpaka mʼmwamba linali masentimita 134.+ 2 Anapanganso nyanga mʼmakona ake 4. Nyanga zake anazipangira kumodzi ndi guwalo.* Atatero anakuta guwalo ndi kopa.*+ 3 Kenako anapanga ziwiya zonse zogwiritsa ntchito paguwalo. Anapanga ndowa, mafosholo, mbale zolowa, mafoloko aakulu ndi zopalira moto. Ziwiya zake zonse anazipanga ndi kopa. 4 Guwalo analipangiranso sefa wa zitsulo zakopa. Analowetsa sefayo chapakati pa guwa lansembe, mʼmunsi mwa mkombero. 5 Analipangiranso mphete 4 mʼmakona ake 4 kuti muzilowa ndodo zonyamulira. Mphetezo anazilumikiza pafupi ndi sefa wa zitsulo zakopa. 6 Kenako anapanga ndodo zonyamulira za mtengo wa mthethe, ndipo anazikuta ndi kopa. 7 Ndodozo anazilowetsa mumphetezo mʼmbali mwa guwa kuti zikhale zonyamulira guwalo. Guwa limenelo analipanga ngati bokosi lamatabwa losatseka pansi.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena