9 Nsembe iliyonse yambewu imene yaphikidwa mu uvuni kapena mʼchiwaya+ izikhala ya wansembe amene wapereka nsembeyo. Izikhala yake.+ 10 Koma nsembe yambewu iliyonse yothira mafuta+ kapena yosathira mafuta+ izikhala ya ana onse aamuna a Aroni, azigawana mofanana.