Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 10:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Choncho malire a dziko la Akanani anachokera ku Sidoni mpaka ku Gerari+ kufupi ndi Gaza,+ nʼkukafika ku Sodomu ndi Gomora+ mpakanso ku Adima ndi Zeboyimu,+ kufupi ndi Lasa.

  • Genesis 15:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Pa tsiku limeneli Yehova anachita pangano ndi Abulamu+ kuti: “Dziko ili ndidzalipereka kwa mbadwa* zako,+ kuyambira kumtsinje wa ku Iguputo mpaka kumtsinje waukulu, mtsinje wa Firate.+

  • Genesis 17:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Dziko limene ukukhalamo ngati mlendoli,+ ndidzalipereka kwa iwe ndi mbadwa zako. Dziko lonse la Kanani lidzakhala lawo mpaka kalekale, ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo.”+

  • Deuteronomo 4:38
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 38 Anachotsa pamaso panu mitundu yaikulu ndi yamphamvu kuposa inu, kuti akulowetseni mʼdziko lawo nʼkukupatsani kuti likhale cholowa chanu ngati mmene zilili lero.+

  • Yoswa 1:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Dziko lanu lidzayambira kuchipululu kufika ku Lebanoni mpaka kumtsinje waukulu wa Firate, dziko lonse la Ahiti+ mpaka kukafika ku Nyanja Yaikulu* kumadzulo.+

  • Yoswa 14:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Aisiraeli anatenga cholowa chawo mʼdziko la Kanani. Wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni ndi atsogoleri a mafuko a makolo a Aisiraeli ndi amene anawagawira cholowachi.+

  • Yeremiya 3:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Ine ndinkaganiza kuti, ‘Mosangalala ndinakuika pakati pa ana aamuna nʼkukupatsa dziko labwino kwambiri, cholowa chokongola kwambiri pakati pa mitundu ya anthu!’*+ Ndinkaganizanso kuti uzindiitana kuti, ‘Bambo anga!’ ndiponso kuti sudzasiya kunditsatira.

  • Machitidwe 17:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Ndipo kuchokera mwa munthu mmodzi+ anapanga mitundu yonse ya anthu, kuti akhale padziko lonse lapansi.+ Iye anaika nthawi yoti zinthu zina zizichitika komanso anaika malire a malo oti anthu azikhala.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena