Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mbiri 15:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Aisiraeli onse ankapita limodzi ndi likasa la pangano la Yehova akufuula mokondwera+ ndiponso akuliza nyanga za nkhosa ndi malipenga.+ Iwo ankaimbanso mokweza zinganga, zoimbira za zingwe ndi azeze.+

  • 2 Mbiri 5:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Alevi onse oimba+ a mʼgulu la Asafu,+ Hemani,+ Yedutuni+ ndiponso ana awo ndi abale awo, anavala zovala zabwino kwambiri atanyamula zinganga, zoimbira za zingwe ndi azeze ndipo anaimirira kumʼmawa kwa guwa lansembe pamodzi ndi ansembe okwana 120 oimba malipenga.+

  • 2 Mbiri 7:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Ansembe anali ataimirira pamalo awo a ntchito. Nawonso Alevi anaimirira pamalo awo ndipo ananyamula zipangizo zoimbira Yehova nyimbo.+ (Mfumu Davide anapanga zipangizo zimenezi kuti azizigwiritsa ntchito poyamikira Yehova komanso pomutamanda kudzera mwa iwowo,* “chifukwa chikondi chake chokhulupirika chidzakhalapo mpaka kalekale.”) Ansembe ankaimba malipenga+ mokweza patsogolo pawo, Aisiraeli onse ataimirira.

  • Ezara 3:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Anthu amene ankamanga nyumbayo anamaliza kumanga maziko a kachisi wa Yehova.+ Atatero, ansembe ovala zovala zaunsembe omwe ananyamula malipenga+ ndiponso Alevi, ana a Asafu omwe ananyamula zinganga, anaimirira kuti atamande Yehova motsatira dongosolo limene Davide mfumu ya Isiraeli anakhazikitsa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena