Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yoswa 1:14, 15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Akazi anu ndi ana anu atsale limodzi ndi ziweto zanu kutsidya lino la Yorodano,+ pamalo amene Mose wakupatsani. Koma asilikali amphamvu nonsenu,+ muwoloke ndipo muzikayenda patsogolo pa abale anu,+ mutakonzeka kumenya nkhondo. Muyenera kuwathandiza. 15 Yehova akadzapereka mpumulo kwa abale anu, ngati mmene waperekera kwa inu, nawonso abale anu akakatenga malo amene Yehova Mulungu akuwapatsa, mʼpamene inuyo mudzabwerere. Mudzabwerera kumalo anu amene Mose mtumiki wa Yehova wakugawirani, tsidya lino la Yorodano, kumʼmawa kuno.’”+

  • Yoswa 22:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Panopa Yehova Mulungu wanu wapatsa abale anu mpumulo mogwirizana ndi zimene anawalonjeza.+ Choncho bwererani, mupite kumatenti anu kudera limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, kutsidya lina* la Yorodano.+

  • Yoswa 22:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Anawauza kuti: “Bwererani kumatenti anu ndi chuma chambiri, ziweto zambiri, siliva, golide, kopa, zitsulo ndi zovala zambiri.+ Tengani katundu amene munakatenga+ kwa adani anu ndipo mukagawane ndi abale anu.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena