15 “Ndikukubweretserani mtundu wa anthu kuchokera kutali, inu a mʼnyumba ya Isiraeli,”+ akutero Yehova.
“Umenewu ndi mtundu umene wakhalapo kwa nthawi yaitali,
Ndi mtundu wakale kwambiri,
Mtundu umene chilankhulo chake simukuchidziwa,
Ndipo simungamve zimene amalankhula.+