-
Levitiko 3:3-5Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Azipereka mbali ina ya nsembe yamgwirizanoyo ngati nsembe yowotcha pamoto yoperekedwa kwa Yehova.+ Azipereka mafuta+ okuta matumbo ndi mafuta onse amene ali pamatumbo. 4 Aziperekanso impso ziwiri ndi mafuta okuta impsozo omwe ali pafupi ndi chiuno. Koma mafuta apachiwindi aziwachotsa pamodzi ndi impsozo.+ 5 Kenako ana a Aroni aziwotcha zinthu zimenezi paguwa lansembe, pamwamba pa nsembe yopsereza yomwe ili pankhuni zimene zili pamoto.+ Imeneyi ndi nsembe yowotcha pamoto yakafungo kosangalatsa* yoperekedwa kwa Yehova.+
-