-
2 Mbiri 5:11-14Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
11 Pamene ansembe anatuluka mʼmalo oyera (chifukwa ansembe onse amene analipo anali atadziyeretsa,+ mosatengera magulu awo),+ 12 Alevi onse oimba+ a mʼgulu la Asafu,+ Hemani,+ Yedutuni+ ndiponso ana awo ndi abale awo, anavala zovala zabwino kwambiri atanyamula zinganga, zoimbira za zingwe ndi azeze ndipo anaimirira kumʼmawa kwa guwa lansembe pamodzi ndi ansembe okwana 120 oimba malipenga.+ 13 Pamene anthu oimba malipenga ndi oimba pakamwa ankaimba mogwirizana potamanda ndi kuthokoza Yehova, pamene mawu a malipenga, zinganga ndi zoimbira zina ankamveka, komanso pamene ankatamanda Yehova ndi mawu akuti, “chifukwa iye ndi wabwino, chikondi chake chokhulupirika chidzakhalapo mpaka kalekale,”+ mtambo unadzaza nyumbayo, nyumba ya Yehova.+ 14 Chifukwa cha mtambowo, ansembewo analephera kupitiriza kutumikira popeza ulemerero wa Yehova unadzaza nyumba ya Mulungu woona.+
-