Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mbiri 30:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Mukabwerera kwa Yehova, abale anu ndi ana anu adzachitiridwa chifundo ndi anthu amene anawagwira+ ndipo adzawalola kubwerera mʼdzikoli.+ Chifukwa Yehova Mulungu wanu ndi wachisomo komanso wachifundo+ ndipo sadzayangʼana kumbali mukabwerera kwa iye.”+

  • Ezara 7:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Iye wandisonyeza chikondi chokhulupirika pamaso pa mfumu,+ pamaso pa alangizi ake+ ndiponso pamaso pa akalonga onse amphamvu a mfumu. Ineyo ndinalimba mtima* chifukwa dzanja la Yehova Mulungu wanga linkandithandiza, ndipo ndinasonkhanitsa atsogoleri a Aisiraeli kuti tipitire limodzi.

  • Nehemiya 2:7, 8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Ndiyeno ndinauza mfumu kuti: “Ngati zili bwino ndi inu mfumu, lolani kuti ndipatsidwe makalata okasonyeza kwa abwanamkubwa a tsidya lina la Mtsinje,*+ kuti akandilole kudutsa mpaka ndikafike ku Yuda. 8 Komanso andipatse kalata yopita kwa Asafu amene akuyangʼanira Nkhalango ya Mfumu, kuti akandipatse mitengo yokakonzera mageti a Nyumba ya Chitetezo Champhamvu+ yakukachisi, mpanda wa mzindawo+ ndiponso nyumba imene ndizikakhalamo.” Choncho mfumu inandipatsa makalatawo+ chifukwa Mulungu anandikomera mtima.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena