Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mafumu 21:19-24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Ukamuuze kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Kodi wapha munthu+ nʼkutenganso munda wake?”’+ Ukamuuzenso kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Pamalo amene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo omwewo agalu adzanyambitanso magazi ako.”’”+

      20 Ndiyeno Ahabu anafunsa Eliya kuti: “Wandipeza kodi mdani wanga?”+ Eliya anayankha kuti: “Inde ndakupezani. Mulungu wanena kuti, ‘Chifukwa watsimikiza mtima kuti uchite zoipa pamaso pa Yehova,+ 21 ndikubweretsera tsoka ndipo ndidzaseseratu nyumba yako ndi kupha mwamuna* aliyense wa mʼbanja la Ahabu,+ ngakhalenso ooneka onyozeka ndi ofooka mu Isiraeli.+ 22 Komanso ndidzachititsa nyumba yako kukhala ngati nyumba ya Yerobowamu+ mwana wa Nebati ndiponso nyumba ya Basa+ mwana wa Ahiya, chifukwa chakuti wandikwiyitsa ndiponso wachititsa kuti Aisiraeli achimwe.’ 23 Komanso ponena za Yezebeli, Yehova wanena kuti, ‘Agalu adzamudya Yezebeli mʼmunda wa ku Yezereeli.+ 24 Munthu aliyense wa mʼbanja la Ahabu wofera mumzinda, agalu adzamudya ndipo wofera kutchire, mbalame zidzamudya.+

  • 2 Mafumu 9:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Ukaphe anthu a mʼbanja la mbuye wako Ahabu ndipo ine ndidzabwezera magazi a atumiki anga aneneri ndiponso magazi a atumiki onse a Yehova amene Yezebeli anawapha.+

  • 2 Mafumu 9:36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 36 Anthuwo atabwerera kwa Yehu kukamuuza, iye anati: “Zimenezi zakwaniritsa mawu a Yehova+ amene ananena kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe, akuti: ‘Mʼmunda wa ku Yezereeli, agalu adzadya thupi la Yezebeli.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena