Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Samueli 24:10-14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Koma Davide atawerenga anthuwo, anayamba kuvutika mumtima mwake.*+ Choncho Davide anauza Yehova kuti: “Ndachimwa+ kwambiri pochita zimenezi. Chonde Yehova, ndikhululukireni tchimo langa ine mtumiki wanu,+ chifukwa ndachita zopusa kwambiri.”+ 11 Davide atadzuka mʼmawa, Yehova anauza mneneri Gadi,+ wamasomphenya wa Davide, kuti: 12 “Pita, ukamuuze Davide kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Pali zilango zitatu zimene ndingakupatse ndipo iwe usankhepo chimodzi.”’”+ 13 Choncho Gadi anapita kwa Davide nʼkumuuza kuti: “Kodi mʼdziko lanu mugwe njala zaka 7?+ Kapena muzithawa adani anu kwa miyezi itatu?+ Kapena mʼdziko lanu mugwe mliri masiku atatu?+ Ganizirani mofatsa zoti ndikayankhe kwa amene wandituma.” 14 Davide atamva zimenezo, anauza Gadi kuti: “Zimenezi zikundisowetsa mtendere kwambiri. Kuli bwino ndilangidwe ndi Yehova,+ chifukwa chifundo chake nʼchachikulu,+ koma ndisalangidwe ndi munthu.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena