Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 11:9-12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Atsogoleri a magulu a asilikali 100+ anachitadi zimene wansembe Yehoyada analamula. Choncho, aliyense anatenga asilikali ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene ankafunika kupuma pa Sabata, nʼkupita kwa wansembe Yehoyada.+ 10 Wansembeyo anapatsa atsogoleri a magulu a asilikali 100 aja mikondo ndi zishango zozungulira zimene zinali za Mfumu Davide, zomwe zinali mʼnyumba ya Yehova. 11 Asilikali olondera nyumba yachifumu+ anaima pamalo awo, aliyense atanyamula zida zake, kuyambira kumanja kwa nyumbayo mpaka kumanzere kwa nyumbayo, pafupi ndi guwa lansembe+ ndiponso pafupi ndi nyumbayo. Anazungulira mfumuyo kumbali zonse. 12 Kenako Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumu+ uja nʼkumuveka chipewa chachifumu nʼkuika mpukutu wa Chilamulo cha Mulungu pamutu pake.+ Choncho anamuveka ufumu nʼkumudzoza. Ndiyeno anayamba kuwomba mʼmanja nʼkumanena kuti: “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena