Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Samueli 17:27-29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Davide atangofika ku Mahanaimu, Sobi mwana wamwamuna wa Nahasi wochokera ku Raba+ mzinda wa Aamoni, Makiri+ mwana wa Amiyeli wochokera ku Lo-debara komanso Barizilai+ wa ku Giliyadi wochokera ku Rogelimu, 28 anabweretsa mabedi, mabeseni, miphika, tirigu, balere, ufa, nyemba zikuluzikulu, mphodza, mbewu zina zokazinga, 29 uchi, nkhosa, bata ndiponso tchizi.* Anabweretsa zinthu zimenezi kuti Davide ndi anthu onse amene anali naye adye.+ Iwo ankati: “Anthuwa ali mʼchipululu ndipo ali ndi njala, ali ndi ludzu komanso atopa.”+

  • 2 Samueli 19:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Ndiyeno Barizilai+ wa ku Giliyadi anabwera kudera la Yorodano kuchokera ku Rogelimu kuti adzaperekeze mfumu mpaka kuwoloka mtsinje wa Yorodano.

  • 1 Mafumu 2:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Koma ana a Barizilai+ wa ku Giliyadi uwasonyeze chikondi chokhulupirika. Akhale mʼgulu la anthu amene azidya patebulo lako, chifukwa anandithandiza+ pa nthawi imene ndinkathawa mchimwene wako Abisalomu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena