-
1 Mbiri 9:10-13Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
10 Pagulu la ansembe panali Yedaya, Yehoyaribu, Yakini+ 11 ndi Azariya mwana wa Hilikiya. Hilikiya anali mwana wa Mesulamu, Mesulamu anali mwana wa Zadoki, Zadoki anali mwana wa Merayoti ndipo Merayoti anali mwana wa Ahitubu. Ahitubu anali mtsogoleri wa nyumba* ya Mulungu woona. 12 Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu. Yerohamu anali mwana wa Pasuri ndipo Pasuri anali mwana wa Malikiya. Komanso panali Maasai mwana wa Adieli. Adieli anali mwana wa Yahazera, Yahazera anali mwana wa Mesulamu, Mesulamu anali mwana wa Mesilemiti ndipo Mesilemiti anali mwana wa Imeri. 13 Panalinso abale awo. Onse anali atsogoleri a nyumba ya makolo awo ndipo analipo 1,760. Iwo anali amuna amphamvu ndiponso oyenerera, omwe ankatumikira panyumba ya Mulungu woona.
-