15 Saluni mwana wa Kolihoze, kalonga wa chigawo cha Mizipa,+ anakonza Geti la Kukasupe+ nʼkukhoma denga lake. Anaikanso zitseko, anamphatika ndi mipiringidzo. Anamanganso mpanda wa Dziwe+ la Ngalande kukafika ku Munda wa Mfumu+ ndi ku Masitepe+ ochokera mu Mzinda wa Davide.+