10 Tsoka kwa amene akukhazikitsa malamulo oipa,+
Amene amangokhalira kulemba malamulo opondereza,
2 Kuti asamvetsere mlandu wa anthu osauka
Ndiponso kuti asachitire chilungamo anthu onyozeka amene ali pakati pa anthu anga.+
Amalanda katundu wa akazi amasiye
Komanso katundu wa ana amasiye.+