13 Ndipo cholengedwa chilichonse chakumwamba, padziko lapansi, pansi pa nthaka,+ panyanja, ndi zinthu zonse zammenemo, ndinazimva zikunena kuti: “Mulungu amene wakhala pampando wachifumu+ komanso Mwanawankhosa,+ atamandidwe, alandire ulemu,+ ulemerero komanso mphamvu mpaka kalekale.”+