8 Ukaona munthu wosauka akuponderezedwa ndiponso zinthu zopanda chilungamo zikuchitika mʼdera limene ukukhala, usadabwe nazo.+ Chifukwa munthu waudindoyo akuonedwa ndi wina waudindo waukulu kuposa iyeyo. Ndipo pali enanso amene ali ndi udindo waukulu kuposa onsewo.