Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mbiri 16:8-13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 “Yamikani Yehova,+ itanani pa dzina lake,

      Dziwitsani mitundu ya anthu ntchito zake!+

      9 Muimbireni, muimbireni nyimbo* zomutamanda,+

      Ganizirani mozama* ntchito zake zonse zodabwitsa.+

      10 Nyadirani dzina lake loyera.+

      Mitima ya anthu ofunafuna Yehova isangalale.+

      11 Funafunani Yehova+ ndipo muzidalira mphamvu zake.

      Nthawi zonse muzimupempha kuti akuthandizeni.*+

      12 Kumbukirani ntchito zodabwitsa zimene wachita,+

      Kumbukirani zozizwitsa zake ndi ziweruzo zimene wanena,

      13 Inu mbadwa* za Isiraeli mtumiki wake,+

      Inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.+

  • Salimo 96:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  3 Lengezani ulemerero wake pakati pa anthu a mitundu ina,

      Lengezani ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.+

  • Salimo 145:11, 12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Iwo adzalengeza za ulemerero wa ufumu wanu+

      Komanso adzalankhula za mphamvu zanu,+

      ל [Lamed]

      12 Kuti anthu adziwe za ntchito zanu zamphamvu+

      Ndiponso kukula kwa ulemerero wa ufumu wanu.+

  • Yesaya 12:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Pa tsiku limenelo mudzanena kuti:

      “Yamikani Yehova, itanani pa dzina lake,

      Dziwitsani mitundu ya anthu ntchito zake.+

      Lengezani kuti dzina lake ndi lokwezeka.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena