Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nehemiya 9:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ndiyeno munakhaulitsa Farao, atumiki ake onse ndiponso anthu onse amʼdziko lake powaonetsa zizindikiro ndi zodabwitsa.+ Munachita zimenezi chifukwa munadziwa kuti iwo anachita zinthu modzikuza+ kwa makolo athu. Pamenepa munadzipangira dzina lomwe lilipobe mpaka lero.+

  • Salimo 78:43-51
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 43 Sanakumbukire mmene anasonyezera zizindikiro zake ku Iguputo,+

      Komanso zinthu zodabwitsa zimene anachita mʼdera la Zowani,

      44 Sanakumbukirenso mmene anasandutsira madzi amʼngalande zotuluka mumtsinje wa Nailo kukhala magazi,+

      Moti sanathe kumwa madziwo.

      45 Mulungu anawatumizira ntchentche zoluma kuti ziwasowetse mtendere,+

      Komanso achule kuti awawononge.+

      46 Anapereka zokolola zawo kwa dzombe lowononga,

      Anapereka zipatso za ntchito yawo kwa dzombe lochuluka.+

      47 Anawononga mitengo yawo ya mpesa+

      Komanso mitengo yawo ya mkuyu ndi matalala.

      48 Anapha nyama zawo zonyamula katundu pogwiritsa ntchito matalala,+

      Ndiponso ziweto zawo ndi mphezi.

      49 Anawasonyeza mkwiyo wake woyaka moto,

      Komanso ukali wake ndipo anawabweretsera mavuto,

      Anawatumizira magulu a angelo kuti awabweretsere tsoka.

      50 Mkwiyo wake anaulambulira njira.

      Sanawapulumutse ku imfa,

      Ndipo anawagwetsera mliri.*

      51 Pamapeto pake anapha ana onse oyamba kubadwa a ku Iguputo,+

      Amene ndi chiyambi cha mphamvu zawo zobereka mʼmatenti a Hamu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena