-
Salimo 78:43-51Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
43 Sanakumbukire mmene anasonyezera zizindikiro zake ku Iguputo,+
Komanso zinthu zodabwitsa zimene anachita mʼdera la Zowani,
44 Sanakumbukirenso mmene anasandutsira madzi amʼngalande zotuluka mumtsinje wa Nailo kukhala magazi,+
Moti sanathe kumwa madziwo.
45 Mulungu anawatumizira ntchentche zoluma kuti ziwasowetse mtendere,+
Komanso achule kuti awawononge.+
46 Anapereka zokolola zawo kwa dzombe lowononga,
Anapereka zipatso za ntchito yawo kwa dzombe lochuluka.+
48 Anapha nyama zawo zonyamula katundu pogwiritsa ntchito matalala,+
Ndiponso ziweto zawo ndi mphezi.
49 Anawasonyeza mkwiyo wake woyaka moto,
Komanso ukali wake ndipo anawabweretsera mavuto,
Anawatumizira magulu a angelo kuti awabweretsere tsoka.
50 Mkwiyo wake anaulambulira njira.
Sanawapulumutse ku imfa,
Ndipo anawagwetsera mliri.*
-