7 Munthu amene amakhulupirira Yehova komanso amene amadalira Yehova,
Ndi amene amadalitsidwa.+
8 Iye adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi,
Umene mizu yake imakafika mumtsinje.
Ngakhale dzuwa litawotcha kwambiri iye sadzamva kutentha,
Koma nthawi zonse masamba ake adzakhala obiriwira.+
Ndipo pa nthawi ya chilala sadzada nkhawa,
Kapena kusiya kubala zipatso.