15 Sizingagulidwe ndi golide woyenga bwino,
Ndipo munthu sangapereke siliva kuti apeze nzeru.+
16 Sangazigule ndi golide wa ku Ofiri,+
Kapena mwala wosowa wa onekisi ndi wa safiro.
17 Nzeru sitingaziyerekezere ndi golide komanso galasi,
Ndipo sitingazisinthanitse ndi mbale ya golide woyenga bwino.+
18 Miyala yamtengo wapatali ya korali ndi kulusitalo sitingaiyerekezere nʼkomwe ndi nzeru.+
Ndipo thumba lodzaza ndi nzeru ndi lamtengo wapatali kuposa thumba lodzaza ndi ngale.