Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 39:10-12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Mkaziyo ankalankhula ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, koma iye sanamvere zoti agone pambali pake kapena kuti agone naye. 11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumba kuti akagwire ntchito yake, ndipo mʼnyumbamo munalibe antchito ena. 12 Choncho mkaziyo anagwira malaya a mnyamatayo nʼkumuuza kuti: “Ugone nane basi!” Koma mnyamatayo anangovula malayawo nʼkuwasiya mʼmanja mwa mkaziyo nʼkuthawira panja.

  • Miyambo 6:23, 24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Chifukwa lamulolo ndi nyale,+

      Ndipo malangizo ndi kuwala,+

      Komanso kudzudzula kumene kumathandiza munthu kusintha ndi njira yakumoyo.+

      24 Zidzakuteteza kwa mkazi woipa,+

      Komanso ku lilime lokopa la mkazi wachiwerewere.*+

  • Miyambo 7:4, 5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Nzeru uiuze kuti: “Ndiwe mchemwali wanga,”

      Ndipo kumvetsa zinthu ukutche “mʼbale wanga,”

       5 Kuti zikuteteze kwa mkazi wamakhalidwe oipa,*+

      Ndiponso kwa mkazi wachiwerewere* wolankhula mawu okopa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena