Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Samueli 18:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Kenako atumiki 10 onyamula zida za Yowabu anabwera nʼkudzamalizitsa kupha Abisalomu.+

  • 2 Samueli 20:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Ndiyeno panali munthu wina wosokoneza dzina lake Sheba,+ mwana wamwamuna wa Bikiri,+ wafuko la Benjamini. Iye analiza lipenga la nyanga ya nkhosa nʼkunena kuti: “Ife Davide tilibe naye ntchito ndipo sitingapatsidwe cholowa kuchokera kwa mwana wa Jese.+ Aisiraeli inu, aliyense apite kwa milungu* yake!”+

  • 2 Samueli 20:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Nthawi yomweyo, mayi wanzeruyo anapita nʼkukalankhula ndi anthu onse, ndipo anthuwo anadula mutu wa Sheba mwana wa Bikiri nʼkuuponya kwa Yowabu. Zitatero, Yowabu analiza lipenga la nyanga ya nkhosa ndipo anthu onse anachoka kumzindawo nʼkupita kwawo.+ Yowabu nayenso anabwerera ku Yerusalemu kwa mfumu.

  • 1 Mafumu 2:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Mfumu Solomo inayankha mayi akewo kuti: “Nʼchifukwa chiyani mukupempha kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa Adoniya? Ndiyetu mumupempherenso ufumu,+ popeza iye ndi mkulu wanga+ ndipo wansembe Abiyatara ndi Yowabu+ mwana wa Zeruya+ ali kumbali yake.”

  • 1 Mafumu 2:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Ndikulumbira mʼdzina la Yehova Mulungu wamoyo, amene anandiika pampando wachifumu wa Davide bambo anga komanso amene anachititsa kuti ufumu wanga ukhazikike+ ndiponso kuti pakhale mzere wa banja lachifumu+ mogwirizana ndi zimene analonjeza, lero Adoniya aphedwa.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena