7 Mapazi a munthu amene akuyenda pamwamba pa mapiri pobweretsa uthenga wabwino ndi okongola kwambiri!+
Munthu amene akulengeza za mtendere,+
Amene akubweretsa uthenga wabwino wa zinthu zabwino,
Amene akulengeza za chipulumutso,
Amene akuuza Ziyoni kuti: “Mulungu wako wakhala Mfumu.”+