50 Yehova wanena kuti:
“Kodi kalata yothetsera ukwati+ wa mayi anu amene ndinawathamangitsa ili kuti?
Kapena kodi ndakugulitsani kwa munthu uti amene ndinali naye ngongole?
Inutu munagulitsidwa chifukwa cha zolakwa zanu,+
Ndipo mayi anu anathamangitsidwa chifukwa cha machimo anu.+