Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 60:21, 22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Anthu ako onse adzakhala olungama.

      Adzatenga dzikoli kukhala lawo mpaka kalekale.

      Anthuwo ndi mmera umene ndinadzala,

      Ndiponso ntchito ya manja anga,+ kuti ineyo ndioneke kukongola.+

      22 Wamngʼono adzasanduka anthu 1,000,

      Ndipo wochepa adzasanduka mtundu wamphamvu.

      Ineyo Yehova ndidzapangitsa kuti zimenezi zichitike mofulumira pa nthawi yake.”

  • Yeremiya 30:18, 19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Yehova wanena kuti:

      “Ndikusonkhanitsa anthu amʼmatenti a Yakobo amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina,+

      Ndipo ndidzamvera chisoni malo okhala a Yakobo.

      Mzinda udzamangidwanso pamalo amene unali poyamba,+

      Ndipo nsanja yokhala ndi mpanda wolimba idzakhala pamalo ake oyenerera.

      19 Kwa iwo kudzamveka mawu oyamikira ndi phokoso la kuseka kwa anthu.+

      Ndidzawachulukitsa moti sadzakhala ochepa.+

      Ndidzawachititsa kuti akhale ambiri,*

      Ndipo sadzakhala anthu ochepa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena