-
2 Mbiri 36:15, 16Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
15 Yehova Mulungu wa makolo awo anapitiriza kuwachenjeza kudzera mwa atumiki ake. Ankawachenjeza mobwerezabwereza chifukwa ankamvera chisoni anthu akewo ndiponso malo ake okhala. 16 Koma iwo anapitiriza kunyoza atumiki a Mulungu woona,+ kunyoza mawu ake+ ndiponso kuseka aneneri ake.+ Iwo anafika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa. Kenako Yehova anawakwiyira kwambiri nʼkuwalanga.+
-
-
Ezekieli 9:9, 10Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
9 Iye anandiyankha kuti: “Zolakwa za nyumba ya Isiraeli ndi Yuda nʼzazikulu kwambiri.+ Dziko lawo ladzaza ndi kukhetsa magazi+ ndipo mumzindamo mwadzaza zinthu zopanda chilungamo.+ Iwo akunena kuti, ‘Yehova wachokamo mʼdziko muno ndipo Yehova sakuona.’+ 10 Koma ine diso langa silimva chisoni ndipo sindiwasonyeza chifundo.+ Ndiwabwezera mogwirizana ndi zochita zawo.”
-