26 Chifukwa pakati pa anthu anga pali anthu oipa.
Iwo amabisala nʼkumayangʼanitsitsa ngati mmene amachitira wosaka mbalame.
Amatchera msampha wakupha
Ndipo amagwira anthu.
27 Mofanana ndi chikwere chimene chadzaza mbalame,
Nyumba zawo zadzaza chinyengo.+
Nʼchifukwa chake iwo ali amphamvu komanso alemera kwambiri.
28 Iwo anenepa ndipo asalala.
Akuchita zinthu zoipa zambiri.
Iwo saweruza mlandu wa ana amasiye mwachilungamo,+
Pofuna kupeza phindu.
Ndipo sachitira chilungamo anthu osauka.’”+