11 Koma Yehova anali nane ngati msilikali woopsa.+
Nʼchifukwa chake anthu amene akundizunza adzakhumudwa ndipo sadzapambana.+
Adzachita manyazi kwambiri chifukwa zinthu sizidzawayendera bwino.
Manyazi awo adzakhala nawo mpaka kalekale ndipo sadzaiwalika.+