Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 3:8, 9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Nditaona zimenezo, ndinathamangitsa Isiraeli wosakhulupirikayo ndipo ndinamupatsa kalata yotsimikizira kuti ukwati watha+ chifukwa anachita chigololo.+ Koma Yuda mchemwali wake, amene ndi wachinyengo, sanachite mantha. Nayenso anayamba kuchita uhule.+ 9 Iye ankaona kuti kuchita uhulewo si vuto moti anapitiriza kuipitsa dzikolo ndipo ankachita chigololo ndi miyala komanso mitengo.+

  • Yeremiya 5:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Kodi ndingakukhululukire bwanji zinthu zimenezi?

      Ana ako aamuna andisiya,

      Ndipo amalumbira pa zinthu zimene si Mulungu.+

      Ndinkawapatsa zimene ankafunikira,

      Koma anapitiriza kuchita chigololo,

      Ndipo ankapita kunyumba ya hule mʼchigulu.

  • Yeremiya 13:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Chigololo chimene ukuchita,+ kumemesa* kwako,

      Khalidwe lako lonyansa* la uhule, zonsezi zidzaonekera.

      Ndaona khalidwe lako lonyansa+

      Mʼmapiri komanso kuthengo.

      Tsoka kwa iwe Yerusalemu!

      Kodi ukhalabe wodetsedwa mpaka liti?”+

  • Ezekieli 22:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Mwa iwe muli munthu amene amachita zonyansa ndi mkazi wa mnzake.+ Wina amadetsa mpongozi wake wamkazi pochita naye khalidwe lonyansa+ ndipo wina amagona ndi mchemwali wake, mwana wamkazi wa bambo ake enieni.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena