-
2 Mafumu 25:8-10Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
8 Mʼmwezi wa 5, pa tsiku la 7 la mweziwo, chomwe chinali chaka cha 19 cha Mfumu Nebukadinezara ya ku Babulo, Nebuzaradani+ mkulu wa asilikali olondera mfumu, mtumiki wa mfumu ya Babulo, anabwera ku Yerusalemu.+ 9 Iye anatentha nyumba ya Yehova,+ nyumba ya mfumu,+ nyumba ya munthu aliyense wotchuka+ komanso nyumba zonse za mu Yerusalemu.+ 10 Kenako asilikali onse a Akasidi, omwe anali ndi mkulu wa asilikali olondera mfumu uja, anagwetsa mpanda wonse wa Yerusalemu.+
-