-
Ezekieli 40:20, 21Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
20 Bwalo lakunja linali ndi kanyumba kapageti kamene kanayangʼana kumpoto. Iye anayeza mulitali ndi mulifupi mwake. 21 Kanyumba kapagetiko kanali ndi zipinda zitatu za alonda mbali iliyonse. Miyezo ya zipilala zake zamʼmbali komanso khonde lake, inali yofanana ndi ya kanyumba kapageti koyamba kaja. Kanyumbako kanali mikono 50 mulitali ndi mikono 25 mulifupi.
-