Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 6:12, 13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Moto wapaguwa lansembe uziyaka nthawi zonse. Usamazime. Wansembe aziikapo nkhuni+ mʼmawa uliwonse nʼkuikapo nsembe yopsereza. Akatero aziwotcha mafuta a nsembe yamgwirizano pamotopo.+ 13 Motowo uziyaka nthawi zonse paguwa lansembe. Usamazime.

  • Numeri 18:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Inu nokha ndi amene muzigwira ntchito za ansembe mʼmalo opatulika+ ndi paguwa lansembe,+ kuti ndisadzakwiyirenso+ Aisiraeli.

  • 2 Mbiri 13:10, 11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Koma ife, Mulungu wathu ndi Yehova+ ndipo sitinamusiye. Ansembe athu, omwe ndi mbadwa za Aroni, akutumikira Yehova, ndipo Alevi akuthandiza pa ntchitoyi. 11 Iwo akupereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼmawa uliwonse+ ndi madzulo alionse limodzi ndi mafuta onunkhira.+ Ndipo mikate yosanjikiza*+ ili patebulo la golide woyenga bwino. Komanso madzulo alionse+ amayatsa nyale zomwe zili pachoikapo nyale chagolide.+ Tikuchita zimenezi chifukwa tikukwaniritsa udindo wathu kwa Yehova Mulungu wathu, koma inuyo mwamusiya.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena