-
Yeremiya 22:8, 9Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
8 Anthu ochokera mʼmitundu yambiri adzadutsa pafupi ndi mzindawu ndipo adzafunsana kuti: “Nʼchifukwa chiyani Yehova anachitira mzinda waukuluwu zinthu zimenezi?”+ 9 Ndipo adzayankha kuti: “Chifukwa chakuti anthu amumzindawu anasiya pangano la Yehova Mulungu wawo nʼkuyamba kulambira milungu ina ndiponso kuitumikira.”’+
-
-
Danieli 9:7Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
7 Inu Yehova ndinu wolungama, koma ifeyo tadzibweretsera manyazi* ngati mmene zilili lero. Manyazi agwira amuna a mu Yuda, anthu a ku Yerusalemu ndi anthu onse a ku Isiraeli, amene ali pafupi ndiponso amene ali kutali, kumayiko onse amene munawabalalitsirako chifukwa choti anakuchitirani zinthu zosakhulupirika.+
-