Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 16:24, 25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Kenako Yesu anauza ophunzira ake kuti: “Ngati munthu akufuna kunditsatira, adzikane yekha ndipo anyamule mtengo wake wozunzikirapo* nʼkupitiriza kunditsatira.+ 25 Chifukwa aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzautaya, koma aliyense amene wataya moyo wake chifukwa cha ine adzaupeza.*+

  • Maliko 8:34, 35
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Kenako iye anaitana gulu la anthu limodzi ndi ophunzira ake nʼkuwauza kuti: “Ngati munthu akufuna kunditsatira, adzikane yekha ndipo anyamule mtengo wake wozunzikirapo* nʼkupitiriza kunditsatira.+ 35 Chifukwa aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzautaya. Koma aliyense wotaya moyo wake chifukwa cha ine ndi uthenga wabwino, adzaupulumutsa.+

  • Luka 9:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Kenako anauza onse kuti: “Ngati munthu akufuna kunditsatira, adzikane yekha+ ndipo anyamule mtengo wake wozunzikirapo* nʼkupitiriza kunditsatira tsiku ndi tsiku.+

  • Luka 14:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Aliyense wosanyamula mtengo wake wozunzikirapo* nʼkunditsatira sangakhale wophunzira wanga.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena