-
Maliko 10:41-45Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
41 Ophunzira 10 ena aja atamva zimenezi, anakwiya kwambiri ndi Yakobo komanso Yohane.+ 42 Koma Yesu anawaitana nʼkuwauza kuti: “Inu mukudziwa kuti amene amaoneka ngati* akulamulira anthu a mitundu ina, amapondereza anthu awo ndipo akuluakulu awo amasonyeza mphamvu zawo pa iwo.+ 43 Sizikuyenera kukhala choncho pakati panu. Koma aliyense amene akufuna kuti akhale wamkulu pakati panu akuyenera kukhala mtumiki wanu+ 44 ndipo amene akufuna kuti akhale woyamba pakati panu akuyenera kukhala kapolo wa onse. 45 Chifukwa ngakhale Mwana wa munthu sanabwere kudzatumikiridwa koma kudzatumikira+ ndi kudzapereka moyo wake dipo* kuti awombole anthu ambiri.”+
-