Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 17:17, 18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Yesu anayankha kuti: “Inu mʼbadwo wopanda chikhulupiriro ndi wopotoka maganizo,+ kodi ndikhala nanube mpaka liti? Ndipitirize kukupirirani mpaka liti? Bwera nayeni kuno.” 18 Ndiyeno Yesu anadzudzula chiwandacho ndipo chinatuluka. Nthawi yomweyo mnyamatayo anachira.+

  • Maliko 9:19-27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Iye anayankha kuti: “Inu mʼbadwo wopanda chikhulupiriro,+ kodi ndikhala nanube mpaka liti? Ndipitirize kukupirirani mpaka liti? Bwera nayeni kuno.”+ 20 Choncho iwo anapita naye kwa Yesu. Koma mzimuwo utamuona, nthawi yomweyo unachititsa kuti mwanayo aphuphe. Anagwa pansi nʼkumagubudukagubuduka ndipo ankachita thovu kukamwa. 21 Ndiyeno Yesu anafunsa bambo ake kuti: “Izi zakhala zikumuchitikira kwa nthawi yaitali bwanji?” Bambo a mwanayo ananena kuti: “Kuyambira ali wamngʼono 22 ndipo nthawi zambiri umamugwetsera pamoto komanso mʼmadzi kuti umuwononge. Koma ngati mungathe kuchitapo kanthu, tichitireni chifundo nʼkutithandiza.” 23 Yesu anafunsa bambowo kuti: “Mukuti ‘Ngati mungatheʼ? Chilichonsetu nʼchotheka kwa munthu amene ali ndi chikhulupiriro.”+ 24 Nthawi yomweyo bambo a mwanayo anafuula nʼkunena kuti: “Chikhulupiriro ndili nacho! Limbitsani chikhulupiriro changa!”+

      25 Tsopano Yesu ataona kuti gulu la anthu likuthamangira kwa iwo, anakalipira mzimu wonyansawo kuti: “Iwe mzimu wolepheretsa munthu kulankhula komanso kumva, ndikukulamula, tuluka ndipo usadzalowenso mwa iye.”+ 26 Mwanayo atafuula ndi kuphupha kwambiri, mzimuwo unatuluka ndipo ankaoneka ngati wafa, moti anthu ambiri ankanena kuti: “Wamwalira!” 27 Koma Yesu anamugwira dzanja nʼkumudzutsa ndipo mwanayo anaimirira.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena