-
Luka 18:31-33Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
31 Kenako anatengera pambali ophunzira 12 aja nʼkuwauza kuti: “Tamverani! Tsopano tikupita ku Yerusalemu ndipo zonse zimene zinalembedwa ndi aneneri zokhudza Mwana wa munthu zikakwaniritsidwa.+ 32 Mwachitsanzo, akamupereka kwa anthu a mitundu ina+ ndipo akamuchitira chipongwe,+ kumunyoza komanso kumulavulira.+ 33 Akakamaliza kumukwapula akamupha,+ koma pa tsiku lachitatu iye adzauka.”+
-