Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 18:1-5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Pa nthawi imeneyo, ophunzira anabwera pafupi ndi Yesu nʼkumufunsa kuti: “Ndi ndani kwenikweni amene adzakhale wamkulu kwambiri mu Ufumu wakumwamba?”+ 2 Choncho iye anaitana mwana wamngʼono nʼkumuimika pakati pawo. 3 Kenako anawauza kuti: “Ndithu ndikukuuzani, mukapanda kutembenuka*+ nʼkukhala ngati ana aangʼono, simudzalowa mu Ufumu wakumwamba.+ 4 Choncho aliyense amene adzadzichepetse ngati mwana wamngʼonoyu ndi amene adzakhale wamkulu kwambiri mu Ufumu wakumwamba.+ 5 Ndiponso aliyense amene walandira mwana wamngʼono ngati ameneyu mʼdzina langa walandiranso ine.

  • Maliko 9:33-37
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 33 Kenako anafika ku Kaperenao. Ndiyeno pamene anali mʼnyumba anawafunsa kuti: “Mʼnjira muja mumakangana chiyani?”+ 34 Iwo anangokhala chete, chifukwa mʼnjira amakangana kuti wamkulu ndi ndani pakati pawo. 35 Choncho anakhala pansi nʼkuitana ophunzira 12 aja nʼkuwauza kuti: “Ngati aliyense akufuna kukhala woyamba, ayenera kukhala wotsiriza pa onse ndiponso mtumiki wa onse.”+ 36 Kenako anatenga mwana wamngʼono nʼkumuimika pakati pawo ndipo anamukumbatira nʼkuwauza kuti: 37 “Aliyense amene walandira mwana wamngʼono+ ngati ameneyu mʼdzina langa, walandiranso ine. Ndipo aliyense amene walandira ine, sanalandire ine ndekha, koma walandiranso Mulungu amene anandituma.”+

  • Luka 22:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Kenako anayamba kukangana kwambiri za amene anali wamkulu kwambiri.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena