Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Zekariya 9:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  9 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni* sangalala kwambiri.

      Fuula mokondwera iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu.*

      Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe.+

      Mfumuyo ndi yolungama ndipo ikubweretsa chipulumutso.*

      Ndi yodzichepetsa+ ndipo ikubwera itakwera bulu.

      Ikubwera itakwera mwana wamphongo wa bulu.+

  • Maliko 11:7-10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Anthuwo anabweretsa bulu uja+ kwa Yesu. Kenako anayala malaya awo akunja pabuluyo ndipo iye anakwerapo.+ 8 Komanso anthu ambiri anayala malaya awo akunja mumsewu ndipo ena anadula masamba mʼminda.+ 9 Ndiyeno amene anali patsogolo komanso amene ankabwera mʼmbuyo ankafuula kuti: “Mʼpulumutseni!+ Wodalitsidwa ndi amene akubwera mʼdzina la Yehova!*+ 10 Wodalitsidwa ndi Ufumu wa atate wathu Davide+ umene ukubwerawo! Mʼpulumutseni kumwambamwambako!”

  • Yohane 12:14, 15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Yesu atapeza bulu wamngʼono, anakwera pabuluyo+ mogwirizana ndi Malemba amene amati: 15 “Usaope mwana wamkazi wa Ziyoni. Taona! Mfumu yako ikubwera itakwera mwana wamphongo wa bulu.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena