Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 28:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Choncho iwo anachoka mwamsanga pamandapo ali ndi mantha ndiponso chimwemwe chochuluka ndipo anathamanga kukauza ophunzira ake.+

  • Luka 24:39-41
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 39 Onani manja ndi mapazi angawa, mutsimikize kuti ndine ndithu. Ndikhudzeni muone, chifukwa mzimu ulibe mnofu ndi mafupa ngati anga amene mukuwaonawa.” 40 Pamene ankanena zimenezi, anawaonetsa manja ndi mapazi ake. 41 Koma popeza iwo sankakhulupirirabe chifukwa cha chimwemwe ndi kudabwa, iye anawafunsa kuti: “Kodi muli ndi chakudya chilichonse pano?”

  • Yohane 20:19, 20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Madzulo a tsiku limenelo, limene linali tsiku loyamba la mlungu, ophunzirawo anasonkhana pamodzi. Mʼnyumba imene anasonkhanayo anakhoma zitseko chifukwa ankaopa Ayuda. Koma Yesu analowa nʼkuima pakati pawo ndipo anawauza kuti: “Mtendere ukhale nanu.”+ 20 Atanena zimenezi, anawaonetsa manja ake ndi munthiti mwake.+ Choncho ophunzirawo anasangalala ataona Ambuyewo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena