9 Koma tikuona Yesu, amene anamutsitsa pangʼono poyerekeza ndi angelo.+ Panopa amuveka ulemerero ndi ulemu ngati chisoti chachifumu chifukwa chakuti anafa.+ Chifukwa cha kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu, zimenezi zinamuchitikira kuti alawe imfa mʼmalo mwa munthu aliyense.+