-
Genesis 14:17-20Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
17 Abulamu akubwera kuchokera kumene anagonjetsa Kedorelaomere limodzi ndi mafumu amene anali naye, mfumu ya ku Sodomu inapita kukakumana naye kuchigwa cha Save, kapena kuti chigwa cha Mfumu.+ 18 Ndipo Melekizedeki,+ mfumu ya mzinda wa Salemu,+ anabweretsa mkate ndi vinyo. Iyeyu anali wansembe wa Mulungu Wamʼmwambamwamba.+
19 Kenako anadalitsa Abulamu kuti:
“Mulungu Wamʼmwambamwamba,
Iye amene anapanga kumwamba ndi dziko lapansi, adalitse Abulamu.
20 Atamandike Mulungu Wamʼmwambamwamba,
Amene wapereka okupondereza mʼmanja mwako!”
Ndipo Abulamu anapatsa Melekizedeki chakhumi cha zinthu zonse+ zimene analanda adaniwo.
-