-
1 Samueli 2:27, 28Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
27 Ndiyeno munthu wa Mulungu anapita kwa Eli nʼkumuuza kuti: “Yehova wanena kuti, ‘Kodi ine sindinachititse kuti anthu amʼnyumba ya bambo ako andidziwe pamene anali akapolo kunyumba ya Farao ku Iguputo?+ 28 Pa mafuko onse a Isiraeli ndinasankha kholo lako+ kukhala wansembe wanga, kuti azipita paguwa langa lansembe+ kukapereka nsembe zanyama, azipereka nsembe zofukiza ndiponso kuti azivala efodi pamaso panga. Komanso ndinapatsa nyumba ya kholo lako nsembe zonse zotentha ndi moto za Aisiraeli.+
-