35 Kubwezera ndi kwanga, chilangonso ndi changa.+
Zimenezi zidzachitika pa nthawi yoikidwiratu phazi lawo likadzaterereka,+
Chifukwa tsiku la tsoka lawo layandikira,
Ndipo zowagwera zifika mofulumira.’
36 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake,+
Ndipo adzamvera chisoni atumiki ake+
Akadzaona kuti mphamvu zawo zatha,
Komanso kuti kwangotsala anthu ovutika ndi ofooka.