-
Ekisodo 12:21-23Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
21 Mwamsanga, Mose anaitana akulu onse a Isiraeli+ nʼkuwauza kuti: “Pitani mukasankhire mabanja anu onse ana a ziweto* nʼkuwapha kuti ikhale nsembe ya Pasika. 22 Mukatero mukatenge kamtengo ka hisope* nʼkukaviika mʼbeseni la magazi nʼkuwawaza pafelemu lapamwamba pa chitseko, ndipo ena mwa magaziwo muwawaze pamafelemu awiri amʼmbali mwa khomo. Aliyense asadzatuluke mʼnyumba yake mpaka mʼmawa. 23 Ndiyeno Yehova akamadzapita kukapha Aiguputo ndi mliri, nʼkuona magazi pamafelemu apamwamba pa zitseko zanu ndi mafelemu awiri amʼmbali mwa khomo, Yehova adzapitirira khomo limenelo ndipo sadzalola mliri wa imfa kulowa mʼnyumba zanu.+
-