3 Koma mawu alionse ouziridwa amene amatsutsa zoti Yesu anabwera monga munthu, amenewo si ochokera kwa Mulungu.+ Mawu amenewo ndi ouziridwa ndi wokana Khristu. Munamva kuti wokana Khristuyu adzalankhula mawu amenewo+ ndipo panopa akuwalankhuladi mʼdzikoli.+