Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Machitidwe 22
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Machitidwe

      • Mawu a Paulo odziteteza pamaso pa gulu la anthu (1-21)

      • Paulo anagwiritsa ntchito mwayi wokhala nzika ya Roma (22-29)

      • Khoti Lalikulu la Ayuda linakumana (30)

Machitidwe 22:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Afi 1:7

Machitidwe 22:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Aro 11:1
  • +Mac 21:39
  • +Mac 5:34
  • +Mac 26:4, 5
  • +Aga 1:14; Afi 3:4-6

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    7/15/1996, ptsa. 26-29

Machitidwe 22:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 8:3; 9:1, 2; 26:9-11; 1Ti 1:12, 13

Machitidwe 22:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 9:3-8; 26:13-15

Machitidwe 22:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 26:16

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    10/15/2012, ptsa. 28-29

Machitidwe 22:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 9:17, 18

Machitidwe 22:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Ak 9:1; 15:8; Aga 1:15, 16

Machitidwe 22:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:11; 26:16

Machitidwe 22:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Ak 6:11; 1Yo 1:7; Chv 1:5
  • +Mac 10:43

Machitidwe 22:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 9:26; Aga 1:18

Machitidwe 22:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 9:28, 29

Machitidwe 22:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 8:3

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/15/2007, tsa. 17

Machitidwe 22:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 7:58; 8:1; 1Ti 1:13, 15

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/15/2007, tsa. 17

Machitidwe 22:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 9:15; 13:2; Aro 1:5; 11:13; Aga 2:7; 1Ti 2:7

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    8/1/1987, tsa. 12

Machitidwe 22:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Sa 16:13

Machitidwe 22:24

Mawu a M'munsi

  • *

    Ena amati, “kumukuwa kapena kumuwowoza.”

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    12/15/2001, ptsa. 21-22

    6/15/1990, tsa. 23

Machitidwe 22:25

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 16:37, 38; 23:27

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    3/1/2015, tsa. 12

    12/15/2001, tsa. 22

Machitidwe 22:28

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 16:37

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 184

Machitidwe 22:29

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 25:16

Machitidwe 22:30

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 10:17, 18; Lu 21:12

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Mac. 22:1Afi 1:7
Mac. 22:3Aro 11:1
Mac. 22:3Mac 21:39
Mac. 22:3Mac 5:34
Mac. 22:3Mac 26:4, 5
Mac. 22:3Aga 1:14; Afi 3:4-6
Mac. 22:4Mac 8:3; 9:1, 2; 26:9-11; 1Ti 1:12, 13
Mac. 22:6Mac 9:3-8; 26:13-15
Mac. 22:10Mac 26:16
Mac. 22:13Mac 9:17, 18
Mac. 22:141Ak 9:1; 15:8; Aga 1:15, 16
Mac. 22:15Mac 23:11; 26:16
Mac. 22:161Ak 6:11; 1Yo 1:7; Chv 1:5
Mac. 22:16Mac 10:43
Mac. 22:17Mac 9:26; Aga 1:18
Mac. 22:18Mac 9:28, 29
Mac. 22:19Mac 8:3
Mac. 22:20Mac 7:58; 8:1; 1Ti 1:13, 15
Mac. 22:21Mac 9:15; 13:2; Aro 1:5; 11:13; Aga 2:7; 1Ti 2:7
Mac. 22:232Sa 16:13
Mac. 22:25Mac 16:37, 38; 23:27
Mac. 22:28Mac 16:37
Mac. 22:29Mac 25:16
Mac. 22:30Mt 10:17, 18; Lu 21:12
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Machitidwe 22:1-30

Machitidwe a Atumwi

22 “Anthu inu, abale anga ndi abambo anga, mvetserani mawu anga odziteteza.”+ 2 Atamva kuti akulankhula nawo mʼChiheberi, onse anangoti zii, ndipo iye anati: 3 “Inetu ndine Myuda,+ wobadwira ku Tariso wa ku Kilikiya,+ koma ndinaphunzitsidwa ndi Gamaliyeli+ mumzinda womwe uno. Anandiphunzitsa kutsatira kwambiri Chilamulo cha makolo+ athu. Ndipo ndinali wodzipereka potumikira Mulungu ngati mmene nonsenu mulili lero.+ 4 Ndinkazunza otsatira Njira imeneyi mpaka kuwapha. Ndinkamanga amuna ndi akazi nʼkukawapereka kundende.+ 5 Ndipotu mkulu wa ansembe ndi bungwe lonse la akulu angandichitire umboni. Kwa amenewa nʼkumene ndinapezanso makalata ondiloleza kuti ndikamange abale ku Damasiko. Ndinanyamuka kuti ndikagwire anthu omwe anali kumeneko nʼkuwabweretsa ku Yerusalemu atamangidwa kuti adzapatsidwe chilango.

6 Koma ndili mʼnjira, nditatsala pangʼono kufika ku Damasiko, dzuwa lili pamutu, mwadzidzidzi kunawala kwambiri. Kuwala kumeneku kunali kochokera kumwamba ndipo kunazungulira pamene ine ndinali.+ 7 Ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akuti: ‘Saulo! Saulo! Nʼchifukwa chiyani ukundizunza?’ 8 Ine ndinayankha kuti, ‘Ndinu ndani Mbuyanga?’ Ndipo anandiuza kuti, ‘Ndine Yesu wa ku Nazareti, amene iwe ukumuzunza.’ 9 Amuna amene ndinali nawo anaona kuwalako, koma sanamvetse mawu amene ankalankhula ndi inewo. 10 Ndiye ine ndinati, ‘Nditani Ambuye?’ Ambuyewo anandiuza kuti, ‘Nyamuka ndipo upite ku Damasiko. Kumeneko ukauzidwa zonse zimene zakonzedwa kuti uchite.’+ 11 Koma popeza sindinkatha kuona chilichonse chifukwa cha ulemerero wa kuwalako, anthu amene ndinali nawo aja, anandigwira dzanja mpaka kukafika ku Damasiko.

12 Ndiyeno Hananiya, munthu woopa Mulungu mogwirizana ndi Chilamulo, amene anali ndi mbiri yabwino pakati pa Ayuda onse akumeneko, 13 anabwera. Iye anaima chapafupi nʼkunena kuti: ‘Mʼbale wanga Saulo, yambanso kuona!’ Nthawi yomweyo ndinakweza maso anga nʼkumuona.+ 14 Ndiyeno iye anati: ‘Mulungu wa makolo athu wakusankha kuti udziwe chifuniro chake, uone wolungamayo+ ndiponso umve mawu apakamwa pake. 15 Chifukwa udzakhala mboni yake kwa anthu onse pa zinthu zimene waona komanso kumva.+ 16 Ndiye ukuchedweranji? Nyamuka ubatizidwe nʼkuchotsa machimo ako+ poitanira pa dzina lake.’+

17 Koma nditabwerera ku Yerusalemu+ nʼkuyamba kupemphera mʼkachisi, ndinaona masomphenya. 18 Mʼmasomphenyawo ndinaona Ambuye akundiuza kuti, ‘Tuluka mu Yerusalemu mwamsanga, chifukwa iwo sadzamva uthenga wako wonena za ine.’+ 19 Ndipo ine ndinanena kuti, ‘Ambuye, iwowo akudziwa bwino kuti ndinkapita mʼmasunagoge nʼkumatsekera mʼndende ndiponso kukwapula anthu amene ankakukhulupirirani.+ 20 Komanso pamene Sitefano, mboni yanu ankaphedwa, ine ndinali pomwepo ndipo ndinavomereza. Ndi inenso amene ndinkayangʼanira malaya akunja a anthu amene ankamuphawo.’+ 21 Koma anandiuzabe kuti, ‘Nyamuka, chifukwa ndidzakutumiza kutali kwa anthu a mitundu ina.’”+

22 Iwo ankamumvetsera mpaka pa mawu amenewa. Koma kenako anafuula kuti: “Munthu ameneyu asapezekenso padziko lapansi! Sakuyenera kukhala ndi moyo!” 23 Koma popeza ankafuula komanso kuponya mʼmwamba malaya awo akunja ndi fumbi,+ 24 mkulu wa asilikali analamula kuti alowe naye kumpanda wa asilikali. Iye anati ayenera kumufunsa mafunso kwinaku akumʼkwapula kuti adziwe chimene chachititsa kuti anthu azimukuwiza* choncho. 25 Koma atamugoneka kuti amukwapule, Paulo anafunsa mtsogoleri wa asilikali amene anaima pamenepo kuti: “Kodi malamulo amakulolani kukwapula nzika ya Roma mlandu wake usanazengedwe?”+ 26 Mtsogoleri wa asilikaliyo atamva zimenezi, anapita kwa mkulu wa asilikali nʼkukamuuza kuti: “Mukufuna kuchita chiyani? Munthuyutu ndi nzika ya Roma.” 27 Zitatero mkulu wa asilikaliyo anabwera nʼkunena kuti: “Tandiuza, kodi nʼzoona kuti ndiwe nzika ya Roma?” Iye anati: “Inde.” 28 Mkulu wa asilikaliyo anati: “Ine ndinagula ufulu wokhala nzika ndi ndalama zambiri.” Paulo anati: “Koma ine wanga ndinachita kubadwa nawo.”+

29 Nthawi yomweyo amuna amene ankafuna kumufunsa mafunso, uku akumukwapula, anachoka nʼkumusiya. Nayenso mkulu wa asilikali uja anachita mantha atadziwa kuti munthu amene anamumangayo ndi nzika ya Roma.+

30 Tsiku lotsatira, pofuna kudziwa chenicheni chimene Ayudawo ankamuimbira mlandu, anamutulutsa. Atatero analamula ansembe aakulu ndi Khoti Lalikulu la Ayuda kuti asonkhane. Ndiyeno anabweretsa Paulo nʼkumuimika pakati pawo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena