Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nyimbo ya Solomo 4
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Nyimbo ya Solomo

    • MSULAMI ALI KU YERUSALEMU (3:6–8:4)

Nyimbo ya Solomo 4:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 32:1; De 3:12; Nym 6:5-7

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, tsa. 19

Nyimbo ya Solomo 4:3

Mawu a M'munsi

  • *

    “Khangaza” ndi mtundu wa chipatso. Ena amati chimanga chachizungu.

Nyimbo ya Solomo 4:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 1:10
  • +Ne 3:25; Nym 7:4
  • +2Sa 8:7; 2Mf 11:10

Nyimbo ya Solomo 4:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 7:3

Nyimbo ya Solomo 4:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mla 2:5

Nyimbo ya Solomo 4:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 4:1

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, tsa. 30

    11/15/2006, tsa. 20

    Galamukani!,

    5/8/1989, tsa. 14

Nyimbo ya Solomo 4:8

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “Anti-Lebanoni.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 3:25
  • +De 3:8, 9; Sl 133:3

Nyimbo ya Solomo 4:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 5:18, 19

Nyimbo ya Solomo 4:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 7:12
  • +Nym 1:2, 4
  • +Est 2:12; Nym 1:12

Nyimbo ya Solomo 4:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 16:24
  • +Nym 5:1

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, tsa. 30

    11/15/2006, tsa. 19

Nyimbo ya Solomo 4:12

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, tsa. 32

    11/15/2006, tsa. 20

    11/1/2000, ptsa. 11-12

    11/15/1987, tsa. 25

Nyimbo ya Solomo 4:13

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “paradaiso.”

Nyimbo ya Solomo 4:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yoh 12:3
  • +Yes 43:24
  • +Miy 7:17
  • +Sl 45:8
  • +Eks 30:23, 24, 34; Eze 27:2, 22

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    2/1/2014, tsa. 10

Nyimbo ya Solomo 4:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yer 18:14

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Nyimbo 4:1Nu 32:1; De 3:12; Nym 6:5-7
Nyimbo 4:4Nym 1:10
Nyimbo 4:4Ne 3:25; Nym 7:4
Nyimbo 4:42Sa 8:7; 2Mf 11:10
Nyimbo 4:5Nym 7:3
Nyimbo 4:6Mla 2:5
Nyimbo 4:7Nym 4:1
Nyimbo 4:8De 3:25
Nyimbo 4:8De 3:8, 9; Sl 133:3
Nyimbo 4:9Miy 5:18, 19
Nyimbo 4:10Nym 7:12
Nyimbo 4:10Nym 1:2, 4
Nyimbo 4:10Est 2:12; Nym 1:12
Nyimbo 4:11Miy 16:24
Nyimbo 4:11Nym 5:1
Nyimbo 4:14Yoh 12:3
Nyimbo 4:14Yes 43:24
Nyimbo 4:14Miy 7:17
Nyimbo 4:14Sl 45:8
Nyimbo 4:14Eks 30:23, 24, 34; Eze 27:2, 22
Nyimbo 4:15Yer 18:14
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Nyimbo ya Solomo 4:1-16

Nyimbo ya Solomo

4 “Ndiwe wokongola wokondedwa wanga.

Ndiwe chiphadzuwa.

Maso ako ali ngati maso a njiwa munsalu yako yophimba kumutuyo.

Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi

Zimene zikuthamanga potsika mapiri a ku Giliyadi.+

 2 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe angozimeta kumene,

Zimene zikuchokera kosambitsidwa,

Zonse zabereka mapasa,

Ndipo palibe imene ana ake afa.

 3 Milomo yako ili ngati chingwe chofiira kwambiri,

Ndipo ukamalankhula umasangalatsa.

Masaya ako munsalu yako yophimba kumutuyo

Ali ngati khangaza* logamphula pakati.

 4 Khosi lako+ lili ngati nsanja ya Davide,+

Yomangidwa ndi miyala yokhala mʼmizeremizere,

Pamene akolekapo zishango 1,000,

Zishango zonse zozungulira za amuna amphamvu.+

 5 Mabere ako awiri ali ngati ana awiri a insa

Ngati ana amapasa a insa,+

Amene akudya msipu pakati pa maluwa.”

 6 “Mpaka kunja kutayamba kuwomba kamphepo kayaziyazi ndiponso mpaka mithunzi itachoka,

Ndipita kuphiri la mule

Ndiponso kuzitunda za lubani.”+

 7 “Ndiwe wokongola paliponse, wokondedwa wanga,+

Ndipo ulibe chilema chilichonse.

 8 Tiye tichokere limodzi ku Lebanoni, iwe mkwatibwi wanga,

Tiye tichokere limodzi ku Lebanoni.+

Utsetsereke kuchokera pamwamba pa phiri la Amana,*

Kuchokera pamwamba pa phiri la Seniri, kapena kuti pamwamba pa phiri la Herimoni.+

Utsetsereke kuchokera mʼmapanga a mikango, ndiponso kuchokera kumapiri a akambuku.

 9 Watenga mtima wanga,+ iwe mchemwali wanga, mkwatibwi wanga,

Watenga mtima wanga utangondiyangʼana kamodzi kokha,

Ndiponso ndi mkanda wa mʼkhosi mwako.

10 Chikondi chimene umandisonyeza nʼchokoma,+ iwe mchemwali wanga, mkwatibwi wanga.

Chikondi chimene umandisonyeza nʼchabwino kuposa vinyo,+

Ndipo kununkhira kwa mafuta ako odzola nʼkoposa zonunkhira zamitundu yonse.+

11 Milomo yako imakha uchi wapachisa,+ iwe mkwatibwi wanga.

Uchi ndi mkaka zili kuseri kwa lilime lako,+

Ndipo kafungo konunkhira ka zovala zako kakumveka ngati kafungo konunkhira ka ku Lebanoni.

12 Mchemwali wanga, mkwatibwi wanga, ali ngati munda umene watsekedwa.

Iye ali ngati munda umene watsekedwa, ndiponso ngati kasupe amene watsekedwa.

13 Uli ngati munda* wa mitengo imene nthambi zake zili ndi makangaza ambiri

Umene uli ndi zipatso zabwino kwambiri, maluwa a hena ndi mitengo ya nado,

14 Nado,+ maluwa a safironi, mabango onunkhira,+ sinamoni,+

Komanso mitengo yosiyanasiyana ya lubani, mule, aloye,+

Ndi zonunkhira zonse zabwino kwambiri.+

15 Uli ngati kasupe wamʼmunda, chitsime chamadzi abwino,

Ndiponso timitsinje tochokera ku Lebanoni.+

16 Dzuka, iwe mphepo yakumpoto.

Bwera, iwe mphepo yakumʼmwera.

Womba pamunda wanga.

Kununkhira kwake kufalikire.”

“Wachikondi wanga alowe mʼmunda wake

Kuti adzadye zipatso zake zabwino kwambiri.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena